Chichewa Literature
Chichewa Literature
Kumbutso: Nthano zimayimbidwa kudzera kunyama zosiyanasiyana kuphatikizapo ziweto. Nyamazi zimagwiritsidwa ntchito molingana
ndi makhalidwe ake. Makhalidwe ndi maonekedwe anyamazo ndiwo amafananitsidwa ndi makhalidwe a anthu.
Mutu I: Za Chuma
Atengambali/ampangankhani: Chingaipe
: Mphunzitsi
: Bwatamu; m’modzi mwa ana aja
: Ana
Malo Ochitikira Nkhani: m’mudzi wina m’malire a nkhalango ya M’ndirasadza
: Kusukulu
Page 1
Kumbutso: Azungu atabwera ku Afrika adapitirizabe malonda osinthanitsa ndipo ankachita malonda osinthanitsa minyanga yanjovu ndi
nsalu, mfuti ndi anthu kenako adabweretsa malonda osinthanitsa zinthu ndi makobidi. Azungu ankachitanso malonda ogulitsa anthu omwe
amakakhala akapolo ndipo amakawagulitsa kumaiko akutsidya la nyanja.
Page 2
Amati munthu wakuda sangachite chinthu chodalirika; zochita zamunthu wachikuda ndi zachikunja.
Amati iwo amachita zodalirika komanso zofunika.
Amadziwa kuti anthu akuda ndi olimbika komanso anzeru mwakuti atha kuwapitirira n’chifukwa chake amafuna
kuwapondereza kuti iwo azikhalabe pamwamba nkumawalamulira pantchito.
Amafuna anthu akuda asiye miyambo yawo nkutenegera khalidwe lachizungulo chonsecho zochita zawo n’zopanda pake,
zolaula komanso zosagwirizana ndi chikhalidwe cha anthu akuda.
Adachenjera potizindikiritsa za sukulu nkutibisira kuti nzeru zamaphunziro timachitazo zitha kutithandiza kuti tizichita zinthu patokha.
Akationa kuti munthu wakuda wayamba kuzindikira amamukankhira kukayamba ntchito mmalo moti agwiritse ntchito nzeruzo pa ulimi
wabwino( kuwerengera zogwiritsa ntchito pa ulimiwo komanso kudziwa phindu lambewuzo)
Amati anthu akuda si anthu koma nyama zakutchire choncho adalengedwa kuti azithandiza azungu.
Anthu akuda:
Ankaona azungu ngati mizimu choncho kudali kovuta kuwatsutsa.
Ankati dziko ndi la azungu popeza katundu yemwe ankagwiritsidwa ntchito anali wochokera kwa azungu monga ku Ulaya.
Ankaganiza kuti katundu wawo ngakhalenso zovala zawo sizabwino komanso zawamba.
Ankatamandira anzawo omwe amavala zovala zakunja.
Page 3
Ankatamandira anzawo omwe amavala zovala zakunja.
Kupondereza
Azungu safuna anthu akuda azikhala ozindikira n’cholinga choti aziwapondereza.
Azungu amadziwa kuti anthu akuda ndi olimbika komanso anzeru mwakuti atha kuwapitirira n’chifukwa chake amafuna
kuwapondereza kuti iwo azikhalabe pamwamba nkumawalamulira ndi pantchito
Kusakondana kwa anthu akuda
Kusagwirizana ndikuchitirana nsanje pa ntchito za malonda.
.Kusalolera makampani ena awiri kapena atatu kugwira ntchito imodzi kuti pakhale kupkisana.
.Kusakhudzidwa ndi mavuto a anzawo: Kulemba ana anzawo komanso anthu ndikumawapatsa malipiro ochepa m’maesiteti.
Anthu akuMalawi amakanika kutukula dziko chonsecho zoyenereza ali nazo ndithu.
Anthu aku Malawi atha:
Kutsatira masomphenya a malemu Bingu Wa Mutharika oti, “Dziko la Malawi silosauka poti lili ndi china chilichonse
chothandiza pachitukuko koma umphawi uli ndi anthu omwe safuna kudzipereka pogwira ntchito.
Kuchita ulimi wamthirira (ulimi wangalande) pogwiritsa ntchito nyanja komanso mitsinje yomwe ilipo m’dziko mwawo.
Kusamala zachilengedwe n’kumatsata malamulo azokopa alendo.
Kudzipezera chochita m’malo modikira kulembedwa ntchito yakuofesi.
Kugwiritsa nzeru zozama zomwe aphunzira kusukulu za ukachenjede pantchito yodzilemba okha.
Page 4
Mutu II: HIV/AIDS
Nthano mwachidule
HIV ndi kachilombo kamene kamayambitsa kutha kwa chitetezo chachibadwidwe mnthupi lamunthu. Ena amati kachilomboka kadachita
kupangidwa ndi akatswiri aza sayansi,ena amati kadachokera kunyama ziweto nkhosa ndi ng’ombe,enanso amati munthu ndi nyani
wochedwa chimpazi izi zikusonyeza kuti sikadziwika bwino komwe kadayambira. Kali ndi zizindikiro kakalowa m’thupi mwamunthu
komanso nkopeweka. Kuno kuMalawi anthu adakatulukira mzaka za 1985 komabe kadali katayamba kale.
HIV idadziwika ku Malawi nanga anthu anali ndi maganizo anji panthawiyi
Panthawiyi anthu anali asadatulukire, ankangoti ndi matenda akanyera/kunyentchera moti amataya nthawi nkumapita kwa asing’anga
mpaka ankafa nawo.
Ena ankangoganizirana za ufiti kapena kulodzana pantchito, pabizinesi, paudindo kumpingo kapena kulimbanirana ufumu.
Zizindikiro za HIV/AIDS
Kutsekula m’mimba kawirikawiri
Kunyozoloka kwa tsitsi ngati bweya
Lilime limaoneka lambuu
Kutsokomola pafupipafupi
Kulefuka ndi kuchita thukuta nthawi iliyonse
Kuonda ndi kusanza
Mashingozi
Page 5
Kukhudza magazi amunthu yemwe ali ndi kachilomboka
Kubwerekana malezala
Kugwiritsa ntchito jakisoni m’modzi anthu ambiri
Kugonana ndi akazi kapena amuna ochuluka/ambirimbiri
Pobereka kapena kuyamwitsa amayi atha kumpatsira mwana
Kapewedwe ka HIV/AIDS
Kupewa mchitidwe wachiwerewere
Kukhulupirirana m’banja
Kugwiritsa ntchito makondomu kwa iwo amene sanakwatirane koma sangathe kupirira
Amayi aleke kubereka ngati adziwa kuti ali ndi HIV.
Kumbutso:
Aliyense aziyesetsa kusamalira thupi lake potsatira malangizo a zaumoyo.
Munthu ayenera kukayezetsa magazi kuti adziwe m’mene m’nthupi mwake muliri.
Phukusi lamoyo sakusungira ndi mnzako, umasunga wekha.
Pachina chilichonse pamakambidwa za HIV/AIDS popeza chilichonse gwero lake ndi moyo wathanzi.
Page 6
Maphunziro m’nkhaniyi
Anthu adaonongeka chifukwa cha kusadziwa.
Anthu posadziwa HIV/AIDS ku Malawi, ankayesa kuti ndi nthenda ya Kanyera kapenanso kuti anthu akulodzana
pamaudindo kumpingo ndi kuofesi mwakuti anthu ambiri amapita kwa asing’anga ndipo adamwalira.
Atengambali m’nkhaniyi
Nkhanu
Mbalame wa mtundu wa pumbwa
Njoka
b) Kumtsinje
Komwe nkhanu inkakhala ndipo idamva chisoni ndi kulira kwa mbalame. Nkhanuyo idacheza ndi mbalame pamalopa, idamva
madandaulo ake ndipo idalonjeza kuthetsa vuto la mbalame.
Page 7
Njira yomwe nkhanu idakonza yophera njoka
Idauza Apumbwa kuti itenga nsomba ndikuika m’njira yomwe njoka imadutsa pokalowa kumphako komwe imakhala.
Idati Sisinya ndi zomwe zidzalondole njoka ndikukaipha kumphako komweko.
Njirayi sidali yabwino popeza Sisinya zidapha mbalame zonse mumtengomo.
Maphunziro m’nkhaniyi
Ndi bwino kusamala ndi omwe tikufuna kuti atithandize pamene takumana ndi vuto.
Nkhanu idauza Sisinya kuti ithandize kupha Njoka popeza idaona kuti Sisinya ndi zomwe zingathe kupha Njokayo. Sisinyazo,
m’malo mwake, zidapha mbalame zonse mumtengo wamkuyu.
Chamwini nchamwini
Tidziganizanso mozama pamalangizo omwe tapatsidwa kuti tiwatsatire.Pumbwa adadalira kwambiri nzeru za ena koma
sizinamuthandize.
Mwano
Gweyani adayankha Khungubwe kuti asavutike ndikumumvera chisoni; angotaya nthawi.
Gweyani adayankha mwaukali pamene Khungubwe ankamumvera chisoni kuti adazizidwa.
Gweyani adauza Khungubwe kuti ntchito yake n’kukamba za anthu ena basi.
Adamfunsa Khungubwe kuti anene chomwe anali kudziyesa.
Kuganiza molakwika
Gweyani atamva kuti Khungubwe ali kumumvera chisoni adaganiza kuti Khungubweyo angofuna kuonetsa kuti iye adali pobisala
pabwino ndipo ankangofuna kuchita matama.
Nkhanza
Gweyani adakwera mumtengo n’kukakasulakasula chisa cha Khungubwe.
Ulesi
Gweyani akuonetsa kuti ndi kanyama kaulesi polephera kudzimangira yekha chisa choti adzikhalamo pa nthawi yozizira kapena
yotentha.
Kusadzidalira
Gweyani adali nyama yosadzidalira, imazizidwa ndi chisanu koma simadzimangira yokha pokhala.
Maphunziro
Chisoni chimaphetsa
Page 9
Khungubwe adachitira chisoni Gweyani atazizidwa namulangiza kuti adzimangire pokhala. Gweyani adayankha mwamwano
komanso mwaukali kuti Khungubweyo achite zake ndipo pamene Khungubwe adapitiriza kulangiza Gweyani adamusasulira chisa.
Page 10
idafunsa chomwe chimachititsa Katunduluyo kuti azidandaula chotero.
Kusazindikira:Njovu sidazindikire kuti pamane chule ankalirapo apadali dzenje lalikulu. Iyo idangokhulupirira kuti
pakulira chulepo pali madzi popeza chule salira popanda madzi.
Kupereka malangizo oyipa: Mpheta idapereka malangizo oyipa kwa Katundulu wamkazi
oti njovu idayenera kuphedwa. Njovu sidayenere kuphedwa
popeza sidachitire dala kupha ana a Katundulu.
Kudalira: Katundulu adadalira mpheta yomwe idapereka ganizo loti njovu iphedwe ndipo
adadaliranso chule yemwe adakonza njira yophera njovu.
Kuganiza mwakuya: Chule adaganiza mwakuya pokhala pafupi ndi dzenje lalikulu nkumalira
pofuna kupha njovu. Njovu idagwera m’dzenjemo pamene idalondola
komwe kumalira chuleyo poganiza kuti yapeza madzi poti
inkakhulupirira kuti pamene chule akulira padayenera kukhala madzi.
Maphunziro
Ena amatha kuvulala kapena kufa kumene kamba ka zinthu zochita mwangozi
Njovu idaphedwa pamene idapha ana akalitundulu itatsotsola chisa mwangozi.
Ena akakhala pachisoni sakhala ndi nthawi younguza ngati zomwe anzawo akuwauza ndi zabwino
kapena zoipa.
Katundulu anali pachisoni chachikulu mwakuti adalibe nthawi younguza ngati ganizo lampheta loti njovu iphedwe lidali labwino
kapena ayi. Iye adangovomereza basi.
Page 11
Matanthauzo amawu
Wakutsina khutu ndi mnansi.
Wakuuza nzeru wakukonda ndithu.
Khama lankhwere
Zidauzira udzu ngakhale kuti moto sudayake.
Atengambali/ampangankhani
Nkhwere
Page 12
Mbalame
Kusazindikira
Nkhwere sizidazindikire kuti psipsiti kadali kachirombo chabe komwe kamaoneka ngati moto koma kadalibe moto.
Nkhanza
Nkhwere idapha mbalame pamene mbalame idatsika kuti ikatsimikizire nkhwerezo kuti moto sungayake .
Maphunziro
Kuthandiza kumaphetsa
Mbalame idaphedwa/idafa pamene idasendera pafupi ndi nkhwere kuti ikatsimikizire nkhwerezo kuti moto sungayake popeza psipsiti
kadali kachirombo chabe kamene kakamauluka kamaoneka ngati moto koma kalibe moto.
Page 13
Cholinga cha mwinibulu pomuveka bulu chikopa chankhalamu
Adzioneka ngati nkhalamu, adzithawidwa ndipo adzikadya m’minda mwa anthu kuti anenepe
Atengambali/ampangankhani
.. Bulu
.. Mwinibulu
.. Anthu am’mudzi
.. Bulu wamkazi
Malo ochitikira nkhani
Ku minda ya anthu: komwe bulu ankapita kukadya zakudya
M’balani : mwinibulu amamutsekeramo buluyo m’mawa uliwonse pochokera
kokudya zakudya m’minda ya anthu.
Mkhalango : Kumene munthu ankangodziyedera.
Mmudzi : Komwe anthu ankakhala
Mfundo zazikulu
Kuchenjera: Mwinibulu adali wochenjera. atazindikira kuti akukanika kumpatsa bulu wake
chakudya chokwanira adamuveka chikopa chankhalamu kuti adzikadya m’minda
mwa anthu mosavutikira.
Chinyengo : Bulu ankanyengezera kukhala nkhalamu.
Kudzidalira: Mwinibulu ankagwira ntchito yochapa m’makomo mwa anthu nkumalipidwa.
Nkhanza : Mwinibulu adaganiza mwankhanza pofuna kudyetsera bulu wake mminda mwa anzake.
Ulesi : Mwinibulu adali waulesi posamufunira bulu wake zakudya mpaka adawonda ndi kufooka.
Maphunziro
Kubisa chilengedwe ndi kovuta
Bulu adavala chikopa chankhalamu nkumaopseza anthu, nkumadya zakudya zam’minda mwawo koma atamva kulira kwa bulu
wamkazi pamtunda wautali adayankhira ndipo anthu adamuzindikira kuti ndi bulu osati nkhalamu.
.Kusasamala kumawonongetsa zinthu: mwinibulu adaphetsa bulu wake chifukwa cha kusamusamala pomufunira
zakudya.
Page 15
akadzodzedwe ufumu
Kunyumba za mbalame zosiyanasiyana: Mbalame zinkakhalako ndipo zidapitakonso
pambuyo pa zokambira zoimitsa kulonga
Kadzidzi ufumu
Mfundo zazikulu
Nsanje: Chikhwangwala adachita nsanje ndi kusankhidwa kwa Kadzidzi kuti alongedwe
ufumu.
Kuganiza bwino: Mbalame zidaganiza bwino kuti zisankhe mfumu popeza zimasowa
woweruza milandu zikalakwirana.
Kudzichepetsa: Chikhwangwala adadzitsutsa powutsa chidani pakati Kadzidzi ndi iye ndipo
adaganiza zokapepesa.
Maphunziro
Nsanje sipindula
Chikhwangwala adayimitsa zokonzekera polonga ufumu wa Kadzidzi kamba ka nsanje chabe komabe
adakapepesa atakalipiridwa nkuzindikira kuti adalakwitsa zinthu.
Waminga ndi miyala: m’mene njoka idadutsamo paulendo womwe sidakafike kamba koti
idakandidwa ndi minga komanso idakhulidwa ndi miyala mpaka
idafa.
Mfundo zazikulu
Nkhanza: njoka imaponda nyerere mosasamala ikamapita kosaka zakudya
Kusasamala: njoka idasankha kudzera njira yomwe sinkadutsamo nthawi zonse mwakuti
sidapitirize ulendo wake pamene idakandika ndi minga komanso kukhulika ndi
miyala mpaka kufa.
Kusunga mangawa: Nyerere zidasunga mangawa pamene njoka inkaziponda ndipo itafa
njokayo izo zidapeza mpata wokalipsira.
Maphunziro
Kuchitira zinthu limodzi nkofunika
Nyerere zidakwanitsa kuguza njoka chifukwa zidali limodzi zonse.
Page 17
adatsika nabwerera kumudzi akulira kamba ka imfa ya anzake aja.
Mfundo zazikulu
Chibwana: anyamata ophunzira adaganiza zobwezeretsa moyo wamkango ndipo atatero
mkangowo udawadya onse.
Tsankho : anyamata ena ophunzira sankafuna kuti mnyamata mzawo wosaphunzira apite
nawo kutauni poganiza kuti palibe munthu yemwe angachite naye chidwi
nkumulemba ntchito kutauniko.
Page 18
Kugwiritsa ntchito nzeru molakwika: anyamata ophunzira aja adaganiza zobwezeretsa
moyo wamkango osaganizira makhalidwe a
mkango.
Chikondi: m’modzi mwa anyamata ophunzira aja adalangiza anzake kuti sikunali kwabwino
kuti amusiye mzawoyo paulendowo popeza adakulira naye limodzi. Iye adauza
anzakewo kuti akakapeza ntchito kutauni aliyense adayenera kumuthandiza
kuchokera ku malipiro awo.
Maphunziro
Maphunziro okha opanda nzeru zachibadwidwe ndi chabe.
Anyamata atatu ophunzira aja adasonyeza kusowa nzeru zachibadwidwe popereka moyo kwa
mkango, chilombo chomwe chidawadya chitangolandira moyowo.
Page 19
Chomwe chidachititsa mfumu Njovu kuti itume njovu zonse kunka
kukasaka madzi
M’nkhalngo mudagwa njala yayikulu.
Madzi m’madambo,m’mitsinje ndi m’ngalande adaphwera.
Nyama zazing’ono zidayamba kufa.
Maonekedwe a Nyanjamwezi
Imaoneka ngati paradizo kamba tizilombo tam’madzimo tomwe timaoneka mochititsa kaso.
Vuto lomwe lidadza njovu zitakamwa madzi ku Nyanjamwezi
Nyama zam’madzi zidathyoledwa makosi ndipo zambiri zidafa.
Mfundo zazikulu
Kudzichepetsa
Njovu itamva dandaulo lomwe lidabwera ndi nthumwi ya Nyanjamwezi, kuti njovu zidalakwa
povunduwiza madzi a Nyanjamwezi komanso popha nyama zam’madzi, idapepesa ndipo
idalonjeza kuti mchitidwe umenewo sudzachitikanso.
Kulimba mtima
Kanyama konga Kalulu kadadzipereka kuti kapita kukayankhula ndi Njovu pamene njovu
zidaponda ndi kupha nyama zam’madzi ku Nyanjamwezi. Kanyamaka kadali kakang’ono koma
sikadaope kupita kunkhalango komwe kudali nyama zazikulu.
Nkhanza
Njovu zidavunduwiza madzi a Nyanjamwezi mosasamala ndipo zidapha nyama zam’madzimo
zomwe zimachititsa kuti Nyanjamwezi iziwoneka ngati paradizo.
Kukhulupirika/Kutumika
Njovu zonse zidavomera zopita kukasaka madzi m’malo mwa nyama zazing’ono.
Chikondi
Njovu zidakasaka madzi mwa nyama zazing’ono zimene, zina mwa izo, zidali zitayamba kale kufa.
Maphunziro
Khalidwe labwino limapindulitsa
Njovu idasankhidwa kukhala mfumu kamba ka khalidwe lake labwino lodziwa kusunga nyama
zonse.
Kulimbamtima ndi kwabwino
Kanyama konga Kalululu kadalimba mtima n’kupita kukayankhula ndi Njovu ngati nthumwi ya
Nyanjamwezi pamene nyama zam’madzi zidaphedwa ndi njovu. Mfumu Njovu idapepesa ndipo
idalonjeza kuti mchitidwewu supitirira.
Ndibwino kuwadzudzula ena akachitira zinthu zolakwika
Page 21
Njovu zitavunduwiza madzi komanso zitaponda ndi kupha nyama zam’madzi ku Nyanjamwezi,
nyama zotsala zidakwiya ndipo zidatuma kanyama konga Kalulu kuti kakadzudzule njovu kuti
zidalakwa poteropo.
Ena akaferedwa amachoka mantha nachita zinthu molimba mtima.
Kanyama konga Kalulu kadachoka mantha ndipo kadalimba mtima kuyankhula ndi mfumu Njovu
popeza kadawawidwa mtima ndi imfa ya abale ake, achinansi, ana ndi azimayi.
Page 22
M’nyumba mwa Tsokalida
Momwe Tsokalida ankasunga mikute yake mumtsuko womwe amamangirira kutsindwi.
Mfundo zazikulu
Kusamala zinthu
Tsokalida akakhuta, amasunga mikute yotsala mumtsuko.
Ulesi
Tsokalida ankangopempha mtauni m’malo mopeza ntchito kwa anthu omwe amampatsa zakudyawo.
Maphunziro
Nthawi zina maloto ndi woyipa
Tsokalida adalota akukhankha mkazi wake yemwe adatanganidwa ndi zinthu zina m’malo mosamala
mwana wake, mwakuti adazindikira kuti wamenya mtsuko womwe amasunga mikute yake ndipo
mikuteyo idamugwera.
Page 23
Kupusa kwa nkhandwe
Idyankhira itamva kulira kwa nkhandwe zinzake pamene inali kuusa poyiwala kuti idakhala
mfumu itanamiza nyamazo.
Pamudzi wina
Pamene Nkhandwe idatulukira ikunka nisaka zakudya
Mfundo zazikulu
Kudzidalira
Nkhandwe idapita yokha kukafuna zakudya
Mwini nyumba, yomwe Nkhandwe idabisala ikuthamngitsidwa ndi agalu, ankagwira ntchito
yazopentapenta.
Kudzithandiza
Nkhandwe idathawira m’nyumba ya munthu wazopentapenta pofuna kupulumutsa moyo wake.
Page 24
Chinyengo
Idauza nyama zomwe zimathawa m’nkhalango kamba ka maonekedwe ake obiliwira kuti Mlengi
adayituma kuti idzakhale mfumu yawo popeza zidalibe mfumu.
Maphunziro
Ndi kovuta kubisa chilengedwe
Nkhandwe idanamiza nyama zonse kuti idatumidwa ndi Mlengi kuti idzakhale mfumu pamene
nyama zimayithawa kamba ka maonekedwe ake obiliwira. Ufumu udatheka komabe
Nkhandweyo idaululika kuti ndi nkhandwe pamene idayankhira itamva kulira kwa nkhandwe
zinzake ndipo idaphedwa ndi nyama zija.
Imfa sithawika
Nkhandwe inkathawa agalu kuti ipulumutse moyo wake. Izi zidatheka ndithu koma idaphedwa
ndi nyama zinzake m’nkhalango pamene zidazindikira kuti mfumu yawoyi idangosintha
maonekedwe koma ndi Nkhandwe.
Chinyengo sichikhalitsa:chimawululika
Nkhandwe idanamiza nyama zonse kuti idatumidwa ndi Mlengi kuti idzakhale mfumu pamene
nyama zimayithawa kamba ka maonekedwe ake obiliwira. Ufumu udatheka komabe
Nkhandweyo idaululika kuti ndi nkhandwe pamene idayankhira itamva kulira kwa nkhandwe
zinzake ndipo idaphedwa ndi nyama zija.
Matanthauzo amawu
Mwantambasale; mozemba
Page 25
moti anali kuopa kuti angadzamumenyere mwana wakeyo. Tsiku lina mayiyu adapita kotunga madzi ndipo
adasiya ana onse awiri m’manja mwa mamuna wake namuuza kuti ateteze mwana wawo kwa Moongose.
Mayiyo atangochoka, mamuna wakeyo adachokanso napita kocheza. Mbuvi idatulukira kuti inkulungize
mwana uja koma Moongose adaipha njokayo natsatira mayiyo kuti akamufotokozere nkhaniyi. Mayi uja
ataona magazi pa Moongose adaganiza kuti wapha mwana wake ndipo adakwiya namponyera mtsuko
Moongose. Moongose adafera pompo. Atafika kunyumba adapeza mwana wake ali bwinobwino pambali
pake pali magazi anjoka yomwe Moongose adapha. Mayiyo adalira kamba kokupha mwana wosalakwa
yemwe adaombola mwana wawo ku imfa.
Page 26
mkazi wamunthu owopa Mulungu adali wankhanza popeza adapha Moongose
pongomuganizira kuti adapha mwana wake asadafufuze mokwanira.
Mfundo zazikulu
Mantha
Mkazi wamunthu owopa Mulungu ankangoopa kuti Moongose akadatha kumenya mwana wawo
pamene sizidali chomwecho.
Kusasamala
Makolo a Moongose adamutaya ali wamng’ono
Munthu wowopa Mulungu sadasamale mwana wake pamene mkazi wake adamusiyira udindo
womusamala iye (mkaziyo) atapita kotunga madzi.
Kuganiza molakwika
Mkazi wamunthu woopa Mulungu ankaganiza molakwika kuti Moongose adali wankhanza kamba
kakuti mtundu wakwawo udalinso wankhanza. Izi zidachtitsa kuti aphe Moongose pamene
adamuona ndi magazi pongoganiza kuti adawaphera mwana.
Kuteteza
Moongose adateteza mwana wa munthu woopa Mulungu kunjoka ya mbuvi yomwe
ikadamuzengereza.
Mkazi wamunthu woopa Mulungu adamusiya mwana wake m’manja mwa bamboo ake kuti
amuyang’anire pamene iye ankapita kotunga madzi. Iye ankakayikira Moongose kuti akadatha
kumenya mwana wakeyo.
Page 27
Kudalira
Mkazi wamunthu woopa Mulungu adadalira mamuna wake kuti amusamalira mwawo pamene
iye adapita kukatunga madzi.
Nkhanza
Makolo a Moongose admutaya adakali mwana
Mayi wamunthu woopa Mulungu adapha Moongose pongomuganizira kuti adapha mwana wake
kamba kakuti adali ndi magazi chonsecho Moongose adapha njoka yomwe ikadavulaza mwana
wake.
Maphunziro
Ndibwino kufufuza nkhani tisanapereke chilango
Mayi wamunthu woopa Mulungu adapha Moongose pongomuganizira kuti adapha mwana wake
kamba kakuti adali ndi magazi. Pamene adathamangira kunyumba adapeza kuti mwana wakeyo
ali bwinobwino popanda vuto lililonse.
Zochitika za Pusi
Kukomedwa ndi maulendo kukabwera anzake
Akachoka pakhomo amakhala masiku angapo asanabwere
Kosaka zakudya
Komwe Pusi adapita ndi anzake ndipo adatha masiku angapo asadabwerere pakhomo mpaka
Changa adalowa nkulanda nyumba ya Pusi
Mfundo zazikulu
Page 29
Kuba
Changa adaba nyumba ya Pusi komanso ya Gonondo.
Nkhanza
Changa adaba nyumba ya Pusi komanso ya Gonondo ponena kuti ndi yake popeza sadapezemo
munthu aliyense monga mwa lamulo.
Kupusa
Gonondo ndi Pusi adali opusa chifukwa Vumbwe atakoloweka chikhatho chake paphewa la
Gonondo komanso atayadzamira mano ake angowe m’khosi mwa Changa, nyama ziwirizi
zidaganiza kuti Vumbwe akufuna azimvetsetsa iwo izo zikamafotokoza nkhani yawo chonsecho
Vumbwe ankakonzekera kupha nyama ziwirizi.
Kudalira
Gonondo ndi Changa adadalira Vumbwe kuti aweruza mlandu wawo.
Malamulo oyipa
M’nkhalangomu mudali lamulo loti munthu akasowa malo napeza nyumba mopanda munthu
aliyense, atha kolowa m’nyumbayo nkuyisandutsa yake.
Chikondi
Gonondo ataona kuti papita masiku koma Pusi sakubwera adapita kukaona kunyumba kwa
Pusiyo.
Maphunziro
Ena amagwiritsa ntchito malamulo olakwika polanda zinthu
za eni.
Changa adalanda nyumba ya Pusi komanso ya Gonondo ponena kuti ndi yake popeza
sadapezemo munthu aliyense monga mwa lamulo loti munthu akasowa malo napeza nyumba
yopanda munthu aliyense, atha kolowa m’nyumbayo nkuyisandutsa yake.
Page 30
Mutu XVI: Mnyamata Wolowerera
Nkhani yonse mwachidule
Mu mzinda wina mutagwa njala, zomoyo zambiri kuphatikizapo agalu adasamukamo. Kanjipiti adachoka mu
mzindawu pothawa njalayo nalowerera kudziko lakutali. Kanjipiti adafika pakhomo pa mayi wina amene
sankasamala zakudya; amangoziyika poyera. Kanjipitiyu akalowa m’nyumbamo amadya zakudya zonse
zomwe wazipeza. Tsiku lina atachitanso zimenezi Kanjipiti adamenyedwa ndi anzake panja pa nyumbayo
mwakuti anali ndi mabala thupi lonse. Kumenyedwaku kudachititsa Kanjipiti kudandaula kuti kudali
kwabwino akadakhala kwawo kusiyana ndi kwa eniku. Kanjipiti adabwerera kwawo ndipo anzake
atamufunsa momwe zimakhalira kudziko linalo, iye adangowayankha kuti anthu amadya, akazi amakhala
balalabalala mtauni ndipo mafumu ndi akuluakulu amakhala modzilemekeza namalandira ulemu.
Page 31
Momwe Kanjipiti adavutika ndi njala
Kudziko lakutali
Komwe Kanjipiti adathawira
Komwe Kanjipiti ankadya zakudya za mayi wina osapempha mpaka tsiku lina anzake
adamukong’ontha
Mfundo zazikulu
Bodza
Kanjipiti atabwerera kwawo ndipo anzake atamufunsa momwe zimakhalira kudziko linalo, iye
adangowayankha kuti anthu amadya, akazi amakhala balalabalala mtauni ndipo mafumu ndi
akuluakulu amakhala modzilemekeza namalandira ulemu. Iye adabisa zoti adathawako popeza
anthu anzake adamkong’ontha.
Nkhanza
Anzake a Kanjipiti adammenya mpaka kumuvulaza kamba koti adadya zakudya panyumba ya
mayi wina osapempha.
Maphunziro
Sibwino kungotenga zinthu za eni osapempha
Kanjipitiyu adalowa m’nyumba ya mayi wina yemwe ankangosiya zakudya osasamala ndipo
adadya zakudya zonse zomwe adazipeza koma sadapemphe. Tsiku lina atachitanso zimenezi
Kanjipiti adamenyedwa ndi anzake panja pa nyumbayo mwakuti anali ndi mabala thupi lonse.
Page 32
mwakuti nyama zomwe zimakhala mozungulira phangalo zidadabwa ndipo zidadabwa. Nkhandwe idadziwa
kuti m’phangamo mudali mdani ndipo idathawa.
Kuganiza mwakuya
Mkango utasakasaka zakudya koma osapeza kanthu kwa tsiku lonse, udalowa m’phanga lina
poganiza kuti nyama yomwe ingabwere kudzagona m’phangamo uyidye.
Nkhandwe itafika paphanga n’kuyimba koma popanda yemwe adayankhirako nyimbo yake,
udayankhula ndi phangalo kuti ngati siliyankha iyo ibwerera. Mkango womwe umayembekezera
kuti ugwire Nkhandweyo udayankhira nyimboyi mwakuti nyama zomwe zimakhala mozungulira
phangalo zidachita mantha.
Maphunziro
Nthawi zina tsoka likatsata wina silitha
Mkango udasakasaka chakudya tsiku lonse koma osachipeza. Utafika paphanga udalowa
poganiza kuti udya nyama yomwe ingalowe m’phangamo koma Nkhandwe yomwe imakhala
m’phangamo itabwera idayimba nyimbo moyankhula ndi phangalo ndipo pamene Mkango
udayankhira nyimboyo, Nkhandwe idadziwa kuti mwalowa mdani choncho idathawa.
Page 33
Mutu XVIII: Msilikali Woumba Mbiya
Nkhani yonse mwachidule
M’misiri wina woumba mbiya adalinso chidakwa. Akatsiriza ntchito yake amapita kumowa. Tsiku lina
ataledzera adaphunthwa nagwa nkutemeka pamphumi. Kuchipatala sadamusamale moyenera choncho
pamphumipo padatsala chipsera(chibambi)choonetsa kuti munthuyo adavulala kwambiri. Patapita nthawi,
m’dzikomo mudagwa njala ndipo atapita kutali adakalowa ntchito ya ulonda. Mfumu yakumeneko pomuona
ndi chipseracho idayesa kuti adali katswiri pankhondo chonsecho chipseracho chidali chabala lomwe lidadza
kamba ka kuledzera. Mfumuyo idamukweza udindo woumba mbiyayu mwakuti adapatsidwa ulemu ndi
mphatso zomwe katswiri wankhondo amalandira kotero kuti anzake ankamuchitira nsanje. Poyendera perete
tsiku lina komanso pofuna kudziwa zomwe msilikali aliyense adachitapo kuti akhale katsiwiri wankondo
komanso nkhondo zomwe adamenyapo, mfumuyo idazindikira kuti munthuyu sadali msilikali. Iye adanena
mwachilungamo kuti adali woumba mbiya ndiponso kuti chibambi chomwe chidali pamphumi pake chidadza
kamba ka ngozi. Mfumuyo idalamula kuti alangidwe koma idasintha maganizo ndikumupempha kuti athawe
anzake asadazindikire kuti iye sadali msilikiali popeza akadamupha. Ngakhale iye adapempha mfumuyo kuti
amulole apite kunkhondo kuti akaonetse luso lake, mfumuyo idakana ponena kuti munthu amene
sadaphunzirepo zankhondo sangapite kunkhondo mpaka ataphunzira zankhondozo.
Page 34
Chilungamo: Woumba mbiya adauza mfumu mwachilungamo kuti iye sadali msilikali
ndipo sadamenyepo nkhondo ina iliyonse. Iye ntchito yake idali youmba
mbiya ndipo chipsera chomwe adali nacho (chomwe chidakopa mfumu
nampatsa udindo waukulu) chidadza pamene adagwera mbiyazo.
Chisoni: Mfumu idamvera chisoni msilikali woumba mbiya pamene adaulula
mwachilungamo kuti iye si msilikali koma woumba mbiya pomuchenjeza kuti
achoke mwansanga pakampupo anthu ena asadamuzindikire kuti simsilikali
popeza akadamupha.
Kusazindikira: Mfumu sidazindikire kuti munthu amene adapatsidwa ulemu
waukuluyo sadali katswiri wankhondo ayi koma katswiri woumba
mbiya.
Kudzidalira: M’misiri ankaumba mbiya ndipo m’dzikomo mutagwa njala adapita kutali
komwe adakalowa ntchito yaulonda.
Kudalira: Woumba mbiya adadalira mfumu yakudziko lakutali yomwe idamulemba
ntchito yaulonda.
Kusasamala:
Mfumu sidafufuze mokwanira za woumba mbiya pamene imafuna kumulemba ntchito mpaka
kumupatsa udindo waukulu pakampu ya asilikali pamene iye adalibe zomuyenereza kukhala
paudindowo.
Ogwira ntchito kuchipatala sadamusamale bwino woumba mbiya mwakuti chipsera chachikulu
chidatsala pamphumi pake chomwe chinkasonyeza kuti adavulala kwambiri.
Maphunziro
Ntchito iliyonse imakhala ndi zoyenereza zake.
Ntchito yomwe adalowa woumba mbiya idayenera munthu amene adapitapo kunkhondo kapena kuti
adamenyapo nkhondo.
Ena polemba ntchito safufuza bwino makhalidwe ndi
maluso a anthu.
Mfumu sidafufuze mokwanira za woumba mbiya pamene imafuna kumulemba ntchito mpaka
kumupatsa udindo waukulu pakampu ya asilikali pamene iye adalibe zomuyenereza kukhala
paudindowo.
Pamavuto munthu sasankha ntchito.
Woumba mbiya adakalowa ntchito yaulonda napatsidwa udindo waukulu pakampu ya asilikali
Page 35
chonsecho iye adali katswiri woumba mbiya.
Maonekedwe amapusitsa
Mfumu idapereka udindo waukulu komanso waulemu kwa munthu woumba mbiya pamene adaona
chipsera pamphumi pake poganiza kuti adali katswiri pankhondo.
Page 36
Malo ochitikira nkhani
Pamtengo: Pamene mlenje adapita kukapumula, adagwira mbalame yomwe inali ndi
chitosi chagolide komanso pamene mbalameyi inkakhala
Kwamfumu
komwe mlenje adapita kukanena zambalame yachitosi chagolide ndipo mfumu idamulanda
mbalameyo
Kumenenso mbalame idapulumukira pamene mfumu idatsekulira mbalameyo pamene
mlangizi wake adauza mfumuyo kuti mbalame singakhale ndi chitosi chagolide popeza
imachokera kudzira
M’chikwatu: m’mene mlenje adasunga mbalame yachitosi chagolide kuti isathawe
Mfundo zazikulu
Kuganiza molakwika komanso mopepera
Mfumu idamvera zomwe mlangizi wake adayiuza kuti padalibe chifukwa chowetera mbalameyo
pamene imachokera kudzira ndipo kuti zomwe amanena mlenjeyo zoti chitosi chake ndi chagolide
n’zabodza komanso n’zopanda umboni. Zidali zosatheka mundowe yambalame kupezeka golide.
Mfumu idatsekulira ndi kupulumutsa mbalame yomwe imataya chitosi chagolide pongomvera
malangizo kuchokera kwa mlangizi wake.
Adaganiza zokanena kwamfumu zambalame yachitosi chagolideyo podera nkhawa kuti ena
akamuona nayo akamunenera kwa mfumu. Izi zidachititsa kuti mfumu imulande mbalameyo.
Kuganiza mwanzeru
Mfumu itamulanda mlenje mbalame yachitosi chagolide, idalamula alonda ake kuti ayisamale
mbalameyo poyipatsa zakudya komanso madzi akumwa.
Mlenje adachita chotheka kuti agwire mbalame yomwe inkataya chitosi chagolide.
Mlenje atagwira mbalame adaisunga m’chikwatu chazingwe zokhazokha kuti isathawe.
Kutaya mwayi wopezapeza
Mlenje adalandidwa mbalame yomwe adagwira yekha ndipo akadapindula nayo kamba ka golide
yemwe adali m’chitosi chake. Iye adaganiza zokanena kwa mfumu podera nkhawa kuti wina
akamunenera akamuona nayo. Mfumu idamulanda mbalameyo.
Mfumu idamvera malangizo olakwika a mlangizi wake kuti padalibe chifukwa chowetera
mbalameyo pamene imachokera kudzira ndipo kuti zomwe amanena mlenjeyo zoti chitosi chake
ndi chagolide n’zabodza komanso n’zopanda umboni. Zidali zosatheka mundowe yambalame
kupezeka golide. Izi zidachititsa mfumu kutsekulira ndi kupulumutsa mbalame yomwe idali ndi
chitosi chagolide yemwe akadapindulira mfumuyo.
Page 37
Kuchenjera
Mbalame itangoona kuti yapulumuka idagwetsanso chitosi chagolide kenako idauluka ndipo
kuchokera apo sidaonekenso.
Maphunziro
Anthu ena amachita zolakwika chifukwa choganizira kapena
kumvera zonena za anthu.
Mfumu idamvera zomwe mlangizi wake adayiuza kuti padalibe chifukwa chowetera mbalameyo
pamene imachokera kudzira ndipo kuti zomwe amanena mlenjeyo zoti chitosi chake ndi chagolide
n’zabodza komanso n’zopanda umboni. Zidali zosatheka mundowe yambalame kupezeka golide.
Itamva zimenezi idatsekulira mbalameyo ndipo idauluka osadzabweranso.
Page 38
Inali ndi nyama zosiyanasiyana
Inali yoopsa zedi
Njokaipuma anali olemera kwambiri
Anali ndi antchito ambiri.
Adanyamuka nkumapita kutauni pamodzi ndi antchito ake
Adayenda pangolo paulendo wakutauni
Anali ndi katundu wambiri paulendowu
M’nkhalango ina
Nkhalango yowirira ndi yoopsa m’mene wachuma ndi antchito ake adakhalamo podikira kuti
ng’ombe yomwe idalefuka ndi kutitimira m’matope ipeze bwino
Wantchito wina adatsalamo yekha atalamulidwa ndi Njokaipuma kuti ayang’anire ng’ombe yomwe
idatitimira m’matope ndipo sinkapezabe bwino
Mfundo zazikulu
Mantha
Wantchito yemwe adalamulidwa ndi Njokaipuma kuti ayang’anire ng’ombe yodwala pamalo ena
m’nkhalango, adatsatira mkuluyo tsiku lotsatiralo namunamiza kuti ng’ombeyo yafa chonsecho
idakali moyo. Iye adachita izi kamba kamantha popeza m’nkhalangomo munali moopsa.
Wantchito wa Njokaipuma, yemwe adalamulidwa kuti atsale ayang’anire ng’ombe yodwala
Page 39
mpaka itapeza bwino, adavomera kamba mantha poganizira mawu omwe abwana ake
adayankhula ndipo adanyamuka asadatsirize kuyankhulako.
Kudalira
Njokaipuma ankadalira antchito ake. Antchitowa ankaongolera ngolo yomwe amakwera
komanso kusamala ziweto zake monga ng’ombe zokoka ngolo
Ng’ombe idadalira wantchito wa Njokaipuma yemwe adailondera pamene sinkapezabe bwino
itadikiliridwa kwa masiku angapo pamene idalefuka ndikutitimira m’matope.
Nkhanza
Wanthito wa Njokaipuma adaisiya ng’ombe yodwala yokhayokha m’nkhalango yoopsa.
Njokaipuma adalamula wantchito wake kuti atsale yekhayekha kuti ayang’anire ng’ombe
yodwala m’nkhalango moopsa zedi.
Chikondi
Njokaipuma ndi antchito ake adayidikira ng’ombe yodwala kwa masiku angapo m’nkhalango
moopsa kuti ipeze bwino kenako apitirize ulendo wawo.
Wantchito wa Njokaipuma adalolera kukhala n’kumayang’anira ng’ombe yodwala m’nkhalango
moopsa yekhayekha.
Ng’ombe yodwala itapeza bwino yokhayokha idalondola mkukuluzi wangolo mpaka idakapeza
mbuye wake ngakhale kuti adayisiya ndi wantchito panjira ndipo wantchitoyonso adayithawa.
Chinyengo/bodza
Wantchito wa Njokaipuma yemwe adamusiya kuti ayang’anire ng’ombe yodwala mpaka ipeze
bwino adayisiya ng’ombeyo nakamunamiza bwana wakeyo kuti ng’ombeyo yafa chonsecho inali
idakali moyo.
Maphunziro
Mantha amachititsa bodza.
Wantchito wa Njokaipuma yemwe adamusiya kuti ayang’anire ng’ombe yodwala mpaka ipeze
bwino adayisiya ng’ombeyo nakamunamiza bwana wakeyo kuti ng’ombeyo yafa chonsecho inali
idakali moyo. Iye adachita izi popeza ankaopa kukhala m’nkhalangomo yekha.
Page 40
Mutu XXI: Kwalimba Uta
Nkhani yonse mwachidule
Panali nkhondo yayikulu pakati pa mbalame ndi nyama kamba kolimbirana ufumu. Pena nyama zinkambana
pena mbalame ndizo. Mleme adapezerapo mwayi womakhala mbali yomwe ikupambana kamba ka
maonekedwe ake. Amauza mbalame kuti ndi mbale wawo kamba kakuti ali ndi mapiko. Ndipo akapita kwa
nyama amati ndi mbale wawo kamba kakuti ali ndi manu ndipo thupi lake si lambalame. Mbali zonse ziwiri
zidamtulukira ndipo zidagwirizana kuti zisamlandire konse. Mbalame zidatsindika kuti zikamupeza zimupha
choncho Mleme, kuchokera tsiku limeneli, sayendanso masana kuopa kuphedwa ndi mbalame.
Page 41
Kudalira
Mbalame zimadalira Khungubwe, Kakowa, Katema, Nkhuku, Kadzidzi, Chiombankhanga,
Ngoloma, Nang’omba ndi zina pankhani yokolowola maso anyama ndi kuzozoola.
Maphunziro
Chinyengo chimakhala ndi mathero ndipo chimabweretsa
mavuto
Mleme ankapusitsa mbalame ndi nyama pamene zinali kumenyanira ufumu pomakhala mbali
imene ikuchita bwino(yalimba) pankhondo yambali ziwirizi. Iye amauza mbalame kuti ndi
mbale wawo popeza anali ndi makupe ndipo nyama kuti ndi mbale wawo poti anali ndi manu.
Mbalame zitamtulukira zidagwirizana kuti zimuphe.
Vuto lililonse limakhala ndi njira yothetsera
Mbalame zitagwirizana kuti ziphe mleme, iye adasankha njira yosamayenda masana koma
usiku wokha.
Matanthauzo amawu
Kuzozoola: kujompha ndi kuvulaza
Kukolowola: kuchotsa ndi zala kapena mlomo monga zichitira mabalame
Page 43
malowo adali awo kuchokera kumakolo awo choncho zipeze kwina kodzera. Pomva dandaulolo, mkulu
wanjovuzo adakhutira nalonjeza zotsatira langizo la mbewazo. Langizoli siliodatsatidwe popeza popeza
mfumu italamula kuti anthu atchere misampha yokolera njovu, Njovu yoyang’anira njovu zinzake ndi njovu
zina zotsatira zidagwidwa. Zitavutika zidapempha mbewa kuti ziwathandize ndipo mbewa zidabwera
nkudula zingwe zamisamphayo mwakuti njovuzo zidapulumuka.
Kusanthula nkhani yonse
Madandaulo a mbewa
Zimafa kamba kopondedwa choncho zimapempha njovu kuti zisiye kudzera komwe izo zinkakhala.
Zomwe Njovu zidayenera kuganizira pa madandaulo a mbewa
Kuchepa sikanthu koma khalidwe
Malo ochitikira nkhani
Kubwinja
Komwe Mbewa zinkakhala
Komwe Njovu zinkadzera popita kokumwa madzi
Komwe mbewa zidapondedwa ndi kuphedwa
Komwe njovu yotsogolera ndi zinzake zidagwidwa m’misampha ndipo zidapulumutsidwa ndi
Mbewa
Mfundo zazikulu
Nkhanza
Njovu zidaponda komanso zidapha Mbewa paulendo wokamwa madzi.
Chisoni
Mbewa zidamvera chisoni Njovu zitakodwa m’misampha yomwe anthu adatchera ndipo
zidazipulumutsa.
Kuderera
Njovu zidaderera Mbewa posatsatira pangano loti Njovuzo zisiye kudutsa ku Bwinja popeza
zinkaponda komanso zinkapha Mbewazo.
Kudalira
Mfumu idadalira anthu kuti atchere misampha yokolera Njovu.
Njovu zidsomboledwa ndi Mbewa pamene zidakodwa m’misampha.
Maphunziro
Kunyalanyaza kumapweteketsa.
Page 44
Njovu zidanyalanyaza pangano lomwe zidachita ndi Mbewa kuti zisiya kudzera kubwinja
mwakuti zidakodwa m’misampha.
Vuto lililonse limakhala ndi njira yolithetsera.
Mbewa zidakachonderera Njovu kuti zisiye kudutsa kubwinja pokamwa madzi popeza
zinkaponda ndiponso zinkapha Mbewazo.
Mfumu idalamula anthu am’mudzi mwake kuti atchere misampha yokolera Njovu.
Wina aliyense ndi wofunikira.
Mbewa zidapulumutsa Njovu pamene zidakodwa m’misampha.
Maphunziro
Ena amphamvu ndi oopedwa amagwa/amafa mopusa
kwambiri.
Mkango unali wamphamvu komanso wolusa koma udamvera bodza la Kalulu kuti kunali
Page 46
mkango wina woopsa. Izi zidachititsa kuti Mkangowo utsatire Kalulu kuti ukathane mdaniyo
mapeto ake udafa ndi mgwazo womwe adatchera Kalulu pachitsime, utaona chithunzi chake
chomwe nkudziponya mwamphamvu poyesa kuti udali mkango winawo.
Vuto lingakule bwanji, limakhala ndi njira yolithetsera.
Mkango udasowetsa nyama mtendere koma Kalulu adapeza njira yowuphera.